Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/05 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
km 4/05 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda Apr. 15

“Kodi si zoona kuti masiku ano pali nkhani zambirimbiri zofunika kuzidziwa? [Yembekezani ayankhe.] Komabe, pankhani zonsezo palibe yofunika kwambiri kuposa imene ikufotokozedwa mu lemba ili. [Werengani Yohane 17:3.] Magazini iyi ikufotokoza tanthauzo la mawu akuti ‘moyo wosatha’ ndiponso mmene tingadziwire zimene zingatitsogolere ku moyo umenewo.”

Galamukani! May 8

“Ngakhale kuti Yesu Kristu amadziwika kwambiri mwina kuposa munthu aliyense amene wakhalapo, anthu ambiri amadabwa kuti kodi iyeyu kwenikweni ndi ndani. Kodi mukudziwa kuti ngakhalenso atumwi ake a Yesu anaganizapo zimenezi? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno werengani Marko 4:41.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena pankhani yoti kodi Yesuyo ndi ndani kwenikweni.”

Nsanja ya Olonda May 1

“Munthu amene timamukonda akamwalira, mwachibadwa timafuna kudzamuonanso. Kodi inu simukuvomereza zimenezi? [Yembekezani ayankhe.] Lonjezo la m’Baibulo lakuti akufa adzauka limatonthoza mtima anthu ambiri. [Werengani Yohane 5:28, 29.] Magazini iyi ikufotokoza za nthawi imene akufa adzauka ndiponso amene kwenikweni adzapindule ndi zimenezo.”

Galamukani! May 8

“Makolo ambiri amasankha zimene ana awo ayenera kuonera. Kodi zakhala zikukuvutani kupeza mafilimu abwino oyenera banja lanu? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno werengani Aefeso 4:17.] Magazini iyi ikufotokoza mmene makolo angathandizire ana awo kusankha zosangalatsa zabwino.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena