Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/08 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
km 5/08 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda May 1

“Anthu ena akamaona kuchuluka kwa masoka achilengedwe, amaganiza kuti Mulungu akutilanga. Kodi maganizo anu ndi otani? [Yembekezani ayankhe. Kenako werengani 1 Yohane 4:8.] Nkhani iyi ikufotokoza chifukwa chake sitiyenera kumuimba mlandu Mulungu chifukwa cha mavuto obwera ndi masoka achilengedwe.” Asonyezeni nkhani imene ili pa tsamba 30.

Galamukani! May

Werengani Mateyo 6:10. Kenako funsani kuti: “Kodi mukudziwa kuti chifuniro cha Mulungu cha dziko lapansi n’chiyani? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limanena kuti Mulungu pachiyambi anali nalo cholinga dziko lapansili, ndipo cholingacho sichinasinthe. Nkhani iyi ikufotokoza zimenezi.” Asonyezeni nkhani imene yayambira pa tsamba 10.

Nsanja ya Olonda June 1

“Imodzi mwa nkhani zodziwika bwino m’Baibulo ndi nkhani ya Nowa ndi Chigumula. Kodi mumakhulupirira kuti Chigumula chinachitikadi? [Yembekezani ayankhe.] Zimene Yesu ananena zimasonyeza kuti chinachitikadi. [Werengani Luka 17:26, 27.] Magazini iyi ikufotokoza chifukwa chake tiyenera kukhulupirira kuti Chigumula chinachitikadi ndiponso zimene tikuphunzirapo.”

Galamukani! June

“Kulera mwana ndi kovuta, makamaka akafika zaka zaunyamata, pamene zambiri zimasintha. Kodi mukuganiza kuti makolo angapeze kuti malangizo odalirika? [Yembekezani ayankhe. Kenako werengani Yesaya 48:17, 18.] Magazini iyi ili ndi mfundo zothandiza makolo kulera ana awo mwanzeru.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena