Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/09 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
km 12/09 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda December 1

“Panyengo ino ya Khirisimasi, ambiri amajambula zinthuzi zosonyeza anzeru akum’mawa atatu akupereka mphatso kwa Yesu potengera nkhani ya m’Baibulo iyi. [Werengani Mateyo 2:1, 11.] Kodi mwaona kuti zimene anthuwa amajambula ndi zosiyana ndi zimene Baibulo limanena? [Yembekezani ayankhe.] Nkhaniyi ikufotokoza zimene zinachitikadi.” Aonetseni nkhani imene ili patsamba 31.

Galamukani! December

“Ndikufuna kumva maganizo anu pa zimene Yesu ananena palemba ili. [Werengani Mateyo 5:3.] Popeza kuti pali zipembedzo zambirimbiri, kodi mukuganiza kuti zipembedzo zonse zingatithandize kuthetsa njala yathu yauzimu? [Yembekezani ayankhe.] Nkhaniyi ili ndi mfundo za Baibulo zotithandiza kudziwa mmene tingathetsere njala yathu yauzimu. Aonetseni nkhani imene ili patsamba 12.

Nsanja ya Olonda January 1

“Zipembedzo zosiyanasiyana zimaphunzitsa zinthu zosiyanasiyana pa nkhani ya kumwa mowa. Kodi inuyo mukuganiza kuti Mulungu amawaona bwanji anthu amene amamwa mowa? [Yembekezani ayankhe.] Ngakhale kuti Baibulo limanena kuti nthawi ina Yesu anasintha madzi kukhala vinyo, limanenanso izi. [Werengani Miyambo 23:20a.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanenadi pa nkhani ya mowa.”

Galamukani! January

“M’nthawi yovuta ino, anthu ambiri amapanikizika kwambiri ndi ntchito. Kodi inunso mumaona kuti mumapanikizika? [Yembekezani ayankhe.] Taonani malangizo othandiza awa. [Werengani Mlaliki 4:6.] Magazini iyi ikufotokoza zimene tingachite kuti tizikhala ndi nthawi yogwira ntchito, yocheza ndi banja lathu komanso yopuma. Ilinso ndi malangizo othandiza anthu amene akufunafuna ntchito.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena