Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/12 tsamba 3
  • Timakobidi Tiwiri Tochepa Mphamvu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Timakobidi Tiwiri Tochepa Mphamvu
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Nkhani Yofanana
  • Moyo wa Anthu Akale—Ndalama
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Yehova Amakonda Opatsa Mokondwerera
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Chitsanzo Chabwino—Mkazi Wamasiye Wosauka
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
  • Anaponya Zochuluka Kuposa Onse
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
km 4/12 tsamba 3

Timakobidi Tiwiri Tochepa Mphamvu

Njira imodzi imene tingathandizire pa zinthu za Ufumu ndi kupereka nawo ndalama zothandizira pa ntchito yolalikira padziko lonse. Bwanji ngati timapeza ndalama movutikira?

Nthawi ina Yesu anaona mkazi wamasiye akuponya timakobidi tiwiri tochepa mphamvu moponyamo zopereka m’kachisi. Kukonda Yehova n’kumene kunachititsa mayiyu kupereka “mu umphawi wake, . . . zonse zimene anali nazo, inde zonse zochirikizira moyo wake.” (Maliko 12:41-44) Chifukwa chakuti Yesu anatchula nkhani imeneyi, zikusonyeza kuti zimene mayiyu anapereka zinali zamtengo wapatali kwa Mulungu. Nawonso Akhristu oyambirira sankaona kuti Akhristu olemera okha ndi amene anali ndi udindo wopereka. Mtumwi Paulo anapereka chitsanzo cha anthu a ku Makedoniya. Ngakhale kuti anali pa ‘umphawi wadzaoneni, . . . anapitiriza kupempha mochonderera kwambiri, kuti awapatse mwayi wopereka nawo.’—2 Akor. 8:1-4.

Choncho, tizikumbukira kuti ngati nafenso tingamapereke “timakobidi tiwiri tochepa mphamvu,” pamapeto pake timakobidi tambiri tidzakhala ndalama zambiri. Ndipotu tikamapereka mochokera pansi pa mtima, Atate wathu wakumwamba amene ndi wopatsa, adzasangalala chifukwa “Mulungu amakonda munthu wopereka mokondwera.”—2 Akor. 9:7.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena