Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp20 No. 3 tsamba 6
  • Kodi Mlengi Wathu Amatithandiza Bwanji Kudziwa Malonjezo Ake?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mlengi Wathu Amatithandiza Bwanji Kudziwa Malonjezo Ake?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2020
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • MAWU A MULUNGU AKUPEZEKA M’ZINENERO ZAMBIRI
  • Kodi Baibulo N’chiyani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • ‘Anatsogoleredwa ndi Mzimu Woyera’
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Baibulo Ndi Buku Lochokera kwa Mulungu
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Kodi Baibulo ‘Linauziridwadi Ndi Mulungu’?
    Galamukani!—2017
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2020
wp20 No. 3 tsamba 6
Bwana akuuza sekilitale zoti alembe m’kalata ndipo sekilitaleyo akutaipa pakompyuta.

Mofanana ndi bwana amene amauza sekilitale wake kuti amulembere uthenga winawake, Mulungu anagwiritsa ntchito anthu okhulupirika kuti alembe Malemba Opatulika

Kodi Mlengi Wathu Amatithandiza Bwanji Kudziwa Malonjezo Ake?

Kungoyambira pamene anthu oyamba analengedwa, Mlengi wathu wakhala akugwiritsa ntchito angelo komanso aneneri pouza anthu malonjezo ake. Kuwonjezera pamenepa, iye anasankha kuti uthenga ndi malonjezo ake zilembedwe. Mulungu akutilonjeza kuti m’tsogolomu tidzasangalala. Ndiye kodi masiku ano malonjezo a Mulungu tingawapeze kuti?

Uthenga wochokera kwa Mulungu umapezeka m’Malemba Opatulika. (2 Timoteyo 3:16) Kodi Mulungu anathandiza bwanji aneneri kuti alembe uthenga wake? (2 Petulo 1:21) Mulungu anaika maganizo ake m’mitima ya amuna osiyanasiyana. Kenako iwo analemba maganizo a Mulunguwo. Zimenezi n’zofanana ndi zomwe zimachitika masiku ano. Mwachitsanzo, bwana akafuna kulemba uthenga winawake, amauza sekilitale wake kuti amulembere uthengawo, ndipo ife tikaulandira timaona kuti wachokera kwa bwanayo osati kwa sekilitale wake. Mofanana ndi zimenezi, ngakhale kuti Mulungu anagwiritsa ntchito amuna osiyanasiyana kuti alembe uthenga wake, Mlembi weniweni wa Malemba Opatulika ndi iyeyo.

MAWU A MULUNGU AKUPEZEKA M’ZINENERO ZAMBIRI

Mawu a Mulungu ndi ofunika kwambiri, ndipo iye amafuna kuti anthu onse aziwawerenga ndi kuwamvetsa bwino. Masiku ano, “uthenga wabwino wosatha” ukupezeka mosavuta ku “dziko lililonse, fuko lililonse, ndi chinenero chilichonse.” (Chivumbulutso 14:6) Mulungu wachititsa kuti buku la Malemba Opatulika lathunthu kapena mbali yake ina lipezeke m’zinenero zoposa 3,000, kuposa buku lina lililonse padziko lapansi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena