Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb17 October tsamba 7
  • Muzitumikira Yehova Nthawi Zonse

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzitumikira Yehova Nthawi Zonse
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Tikuphunzira Chiyani pa Fanizo la Matalente?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kulongosola Nkhani za Kugwiritsiridwa Ntchito kwa Ndalama za Kristu
    Chisungiko cha Padziko Lonse mu Ulamuliro wa “Kalonga wa Mtendere”
  • Muzisangalala ndi Utumiki Wanu
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
  • Fanizo la Matalente
    Nsanja ya Olonda​—1990
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
mwb17 October tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzitumikira Yehova Nthawi Zonse

Moyo ndi mphatso ya mtengo wapatali. Zimene timachita tsiku ndi tsiku zimasonyeza ngati timayamikira mphatsoyi kapena ayi. Monga Mboni za Yehova, timayesetsa kugwiritsa ntchito mphamvu zathu komanso luso lathu potumikira Yehova, yemwe anatipatsa moyo. (Sal. 36:9; Chiv. 4:11) Komabe nkhawa za tsiku ndi tsiku zimene timakhala nazo zingasokoneze zolinga zathu zofuna kutumikira Yehova. (Maliko 4:18, 19) Choncho tonsefe tingachite bwino kudzifunsa kuti: ‘Kodi ndikuyesetsa kuchita zonse zimene ndingathe potumikira Yehova? (Hos. 14:2) Kodi ntchito imene ndimagwira ikundilepheretsa kuchita zambiri? Kodi zolinga zanga n’zotani? Kodi ndingatani kuti ndizichita zambiri mu utumiki?’ Ngati mukuona kuti pali zina zimene mukufunikira kusintha, pempherani kwa Yehova kuti akuthandizeni. Musamakayikire kuti kutumikira Yehova nthawi zonse kudzakuthandizani kukhala ndi moyo wabwino komanso wosangalala.​—Sal. 61:8.

Edgardo Franco akuimba; Edgardo Franco ali mu utumiki

Kodi inuyo mumapereka luso lanu kwa ndani?

ONERANI VIDIYO YAKUTI MUZIGWIRITSA NTCHITO LUSO LANU KUTUMIKIRA YEHOVA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • N’chifukwa chiyani tinganene kuti si nzeru kugwiritsa ntchito luso lathu pa zinthu za m’dziko la Satanali? (1 Yoh. 2:17)

  • Kodi anthu amene amachita zonse zimene angathe potumikira Yehova amapeza madalitso otani?

  • Kodi mungathe kugwiritsa ntchito luso lanu pochita mautumiki osiyanasiyana ati?

ZIMENE MUNGACHITE PA KULAMBIRA KWA PABANJA:

  • Funsani wofalitsa amene watumikira Yehova kwa zaka zambiri, mwina pochita utumiki wa nthawi zonse. Kodi anadzimana zinthu ziti kuti azichita zambiri potumikira Yehova? Nanga Yehova wamudalitsa bwanji?

  • Pitani pa JW Broadcasting, ndipo onani pamene alemba kuti ZOCHITIKA PA MOYO WA ANTHU ENA > MADALITSO OBWERA CHIFUKWA CHOCHITA UTUMIKI WA NTHAWI ZONSE. Pamenepo muona komanso kumva zosangalatsa zimene zinachitikira anthu ena amene akhala akuchita mautumiki osiyanasiyana kwa nthawi yaitali

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena