Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb18 May tsamba 4
  • Masomphenya Olimbitsa Chikhulupiriro

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Masomphenya Olimbitsa Chikhulupiriro
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Nkhani Yofanana
  • Mmene Kusandulika kwa Kristu Kumakuyambukirirani
    Nsanja ya Olonda—1991
  • Anaona Ulemelero wa Khristu Atasandulika
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Maulosi a Baibulo Agona pa Kristu
    Nsanja ya Olonda—2005
  • Labadirani Mawu Aulosi a Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2000
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
mwb18 May tsamba 4

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MALIKO 9-10

Masomphenya Olimbitsa Chikhulupiriro

9:1-7

Petulo, Yakobo ndi Yohane akuona Yesu akusandulika

Taganizirani mmene Yesu anamvera pa nthawi ya kusandulika kwake, pamene Atate ake ananena kuti amakondwera naye! N’zosachita kufunsa kuti zimenezi zinamulimbikitsa kuti apirire mayesero omwe ankayembekezera kukumana nawo. Masomphenyawa analimbikitsanso Petulo, Yakobo ndi Yohane. Iwo anaona kuti Yesu ndi Mesiyadi ndipo ankachita bwino kumumvera. Patadutsa zaka 32 kuchokera nthawi imeneyi Petulo anatchula za masomphenya omwe anaonawa ndipo ananena kuti anamulimbikitsa kuti azikhulupirira kwambiri ‘mawu aulosi.’​—2 Pet. 1:16-19.

Ngakhale kuti ifeyo sitinaone nawo masomphenyawa, timaona kukwaniritsidwa kwake masiku ano. Panopa Yesu akulamulira monga Mfumu yamphamvu. Posachedwapa ‘apambana pa nkhondo yolimbana’ ndi adani ake, ndipo zimenezi zidzabweretsa dziko latsopano lolungama.​—Chiv. 6:2.

Kodi kukwaniritsidwa kwa maulosi a m’Baibulo kumalimbitsa bwanji chikhulupiriro chanu?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena