Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb21 July tsamba 11
  • Uziona Akazi Achikulire Ngati Amayi Ako, Akazi Achitsikana Ngati Alongo Ako

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Uziona Akazi Achikulire Ngati Amayi Ako, Akazi Achitsikana Ngati Alongo Ako
  • Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mumaona Akazi Ngati Mmene Yehova Amawaonera?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
  • Muzilimbikitsa Alongo Mumpingo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2020
  • Udindo Umene Akulu Ali Nawo Mumpingo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
  • Muziona Kuti Anthu Ena Ndi Ofunika Mumpingo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2020
Onani Zambiri
Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
mwb21 July tsamba 11
M’bale akuthandiza mlongo wachikulire kukakwera galimoto ndipo mlongo wachitsikana wagwira dzanja la mlongoyo.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Uziona Akazi Achikulire Ngati Amayi Ako, Akazi Achitsikana Ngati Alongo Ako

Malemba amatiuza kuti tiziona Akhristu achikulire ngati amayi ndi abambo athu komanso tiziona Akhristu achinyamata ngati abale athu. (Werengani 1 Timoteyo 5:1, 2.) Makamaka abale, ayenera kumachita zinthu mwaulemu ndi alongo.

M’bale sayenera kukopa kapena kuchita zinthu zomwe zingachititse kuti mlongo asakhale womasuka. (Yob 31:1) M’bale wosakwatira sayenera kuseweretsa maganizo a mlongo wosakwatiwa pomuchititsa kuganiza kuti akufuna kukhala naye pachibwenzi, pomwe m’baleyo alibe maganizo amenewo.

Akulu ayenera kuchita zinthu mokoma mtima ndi alongo omwe afunsa funso kuti adziwe zinazake kapena omwe atchula nkhani inayake yomwe akuluwo angafunike kuisamalira. Akulu ayenera kuchita zinthu moganizira alongo omwe alibe amuna owasamalira.​—Ru 2:8, 9.

ONERANI VIDIYO YAKUTI MUZISONYEZA CHIKONDI CHOSATHA MUMPINGO WACHIKHRISTU​—MUZIKONDA AKAZI AMASIYE NDI ANA AMASIYE, NDIPO KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti ‘Muzisonyeza Chikondi Chosatha Mumpingo Wachikhristu—Muzikonda Akazi Amasiye ndi Ana Amasiye.’ Mwamuna wa Mlongo Myint atachita ngozi abale ndi alongo apita kunyumba kwa mlongoyo kukamutonthoza limodzi ndi ana ake.

    Kodi abale ndi alongo anasonyeza bwanji chikondi chachikulu kwa Mlongo Myint?

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti ‘Muzisonyeza Chikondi Chosatha Mumpingo Wachikhristu—Muzikonda Akazi Amasiye ndi Ana Amasiye.’ Aneba a Mlongo Myint akuona banja la Mboni likupita kukaona mlongoyu ndi ana ake.

    Kodi chikondi chimene abale ndi alongo anasonyeza kwa Mlongo Myint chinathandiza bwanji kuti dzina la Yehova lilemekezedwe?

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti ‘Muzisonyeza Chikondi Chosatha Mumpingo Wachikhristu—Muzikonda Akazi Amasiye ndi Ana Amasiye.’ Mlongo Myint ndi ana ake apita kumisonkhano.

    Kodi chikondi chimene abale ndi alongo anasonyeza kwa Mlongo Myint chinathandiza bwanji ana ake?

Kodi ndi njira zina ziti zimene mungasonyezere kuti mumaganizira alongo mumpingo wanu?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena