Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp25 No. 1 tsamba 4-5
  • Kodi Nkhondo Komanso Zachiwawa Zimatikhudza Bwanji Tonsefe?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Nkhondo Komanso Zachiwawa Zimatikhudza Bwanji Tonsefe?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2025
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Anthu Adzasiya Liti Kumenya Nkhondo?—Zimene Baibulo Limanena
    Nkhani Zina
  • Ndalama Zambirimbiri Zikuthera Kunkhondo—Kodi Ndi Ndalama Zochuluka Bwanji?
    Nkhani Zina
  • Kodi Nkhondo Komanso Zachiwawa Zidzathetsedwa Bwanji?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2025
  • Nkhondo
    Galamukani!—2017
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2025
wp25 No. 1 tsamba 4-5
Zithunzi: 1. Msilikali akuyenda m’munda ndipo kumbuyo kwake kukubwera chigalimoto cha nkhondo. 2. Amuna, akazi komanso ana a mitundu yosiyanasiyana amene akhudzidwa ndi nkhondo.

Kodi Nkhondo Komanso Zachiwawa Zimatikhudza Bwanji Tonsefe?

“Kungoyambira pa nthawi ya nkhondo yachiwiri yapadziko lonse, zachiwawa zakhala zikungowonjezereka ndipo anthu 2 biliyoni, omwe ndi munthu mmodzi pa anthu 4 alionse padzikoli, akukhala m’malo amene kukuchitika zachiwawa.”

Wachiwiri kwa Mlembi Wamkulu Bungwe la United Nations, Amina J. Mohammed, 26 January 2023.

Nkhondo komanso zachiwawa zingayambike mwadzidzidzi m’malo amene panopa muli mtendere. Ngakhale anthu amene ali m’mayiko akutali ndi kumene zimenezi zikuchitika amakhudzidwanso. Ndipo mavuto amene amayambika chifukwa cha nkhondoyo amakhalapo kwa nthawi yaitali ngakhale itatha. Taonani zitsanzo zotsatirazi:

  • Kachithunzi ka manja awiri atagwira mbale yopanda kanthu mkati.

    Kusowa kwa chakudya. Nthambi ya Bungwe la UN yoona za chakudya padziko lonse inanena kuti, “nkhondo ndi zimene zikuchititsa kuti padzikoli anthu ambiri azivutika ndi njala, moti 70 peresenti ya anthu amene akuvutika ndi njala amakhala m’madera amene muli nkhondo komanso zachiwawa.”—World Food Programme.

  • Kachithunzi ka mzimayi wokhumudwa ataphimba nkhope yake ndi manja.

    Mavuto okhudza maganizo komanso thanzi. Anthu akadziwa kuti m’dera lawo mukhoza kuchitika nkhondo amayamba kuda nkhawa komanso kuvutika kwambiri maganizo. Kuwonjezera pa kuvulala, nthawi zambiri anthu a m’madera amene kukuchitika nkhondo amakhalanso ndi mavuto a maganizo. Koma zimakhalanso zovuta kuti alandire thandizo lachipatala.

  • Kachithunzi ka banja litanyamula zikwama zawo.

    Kuthawa nkhondo. Malinga ndi zimene inanena nthambi ya bungwe la United Nations yoona za anthu othawa kwawo (United Nations High Commissioner for Refugees), pofika mu September 2023, anthu oposa 114 miliyoni padziko lonse anakakamizika kuthawa kwawo. Nkhondo komanso zachiwawa ndi zimene zikuchititsa kwambiri vutoli.

  • Kachithunzi ka banja litayima panja pa kanyumba kawo.

    Mavuto azachuma. Nthawi zambiri anthu amakumana ndi mavuto azachuma oyambitsidwa ndi nkhondo monga kutsika mphamvu kwa ndalama. Anthu akhoza kuvutika ngati boma likugwiritsa ntchito ndalama zambiri pa nkhondo m’malo mozigwiritsa ntchito pa zaumoyo komanso maphunziro. Ndipo pamafunika ndalama zambiri zomangiranso zinthu zimene zinawonongedwa pankhondo.

  • Kachithunzi ka mafuta omwe akutuluka mpaipi.

    Kuwonongedwa kwa chilengedwe. Anthu amavutika kwambiri dera lawo likawonongedwa pankhondo. Kuwonongeka kwa madzi, mpweya ndiponso nthaka kumayambitsa matenda osiyanasiyana amene anthu angavutike nawo kwa nthawi yaitali, komanso anthu akhoza kuvulala kapenanso kuphedwa ndi zida zankhondo zimene zinasiyidwa munthaka ngakhale patapita nthawi yaitali kuchokera pamene nkhondo inatha.

N’zosachita kufunsa kuti nkhondo imawonongetsa zinthu zambiri.

Maulosi a m’Baibulo Okhudza Nkhondo

Maulosi a m’Baibulo amasonyeza kuti nkhondo komanso zachiwawa ndi mbali ya chizindikiro cha “mapeto a nthawi ino.” (Mateyu 24:3) Yesu Khristu ananeneratu kuti:

  • “Mudzamva phokoso la nkhondo ndi malipoti a nkhondo. . . . Mtundu udzaukirana ndi mtundu wina ndipo ufumu udzaukirana ndi ufumu wina.”—Mateyu 24:​6, 7.

  • “Mukadzamva phokoso la nkhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha.”—Luka 21:9.

    Mawu oyambirira amene anawamasulira kuti “zipolowe” angatanthauze zipwirikiti, kuukira, kutsutsa boma, kulimbana ndi olamulira, mpungwepungwe pa ndale komanso zionetsero.

Kuti mudziwe zambiri, werengani nkhani yakuti “Kodi Chizindikiro cha ‘Masiku Otsiriza’ Kapena Kuti ‘Nthawi ya Mapeto’ N’chiyani?” pa jw.org.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena