Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w25 October tsamba 32
  • Muzitsatira Ndandanda Yanu Yowerengera Baibulo Tsiku Lililonse

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzitsatira Ndandanda Yanu Yowerengera Baibulo Tsiku Lililonse
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Tingagwiritse Ntchito Bwanji Zinthu Zimene Zinajambulidwa Kuti Tizimvetsera?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Kodi Mukugwiritsa Ntchito Mokwanira Baibulo Longomvetsera?
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Kupindula ndi Kuŵerenga Baibulo Tsiku ndi Tsiku
    Nsanja ya Olonda—1995
  • Kodi Ndingatani Kuti Kuŵerenga Baibulo Kuzindisangalatsa?
    Galamukani!—2001
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
w25 October tsamba 32

MFUNDO ZOTHANDIZA POPHUNZIRA

Muzitsatira Ndandanda Yanu Yowerengera Baibulo Tsiku Lililonse

Kodi zimakuvutani kutsatira ndandanda yanu yowerengera Baibulo tsiku ndi tsiku chifukwa chakuti mumakhala otanganidwa? (Yos. 1:8) Ngati ndi choncho, yesani kuchita chimodzi mwa zinthu zotsatirazi:

  • Muzitchera alamu. Mungatchere alamu pafoni yanu kapena pachipangizo chinachake kuti izikukumbutsani kuwerenga Baibulo.

  • Muziika Baibulo lanu pamalo oonekera. Ngati mumagwiritsa ntchito Baibulo lochita kupulinta, muziliika pamalo oti muzitha kuliona tsiku lililonse.—Deut. 11:18.

  • Muzimvetsera Baibulo lochita kujambulidwa. Mukhoza kumamvetsera Baibulo pa nthawi imene mukugwira ntchito zanu za tsiku ndi tsiku. Tara yemwe ndi mpainiya, ali ndi ana komanso amagwira ntchito usiku ananena kuti, “Kumvetsera Baibulo lochita kujambulidwa uku ndikugwira ntchito zapakhomo, kumandithandiza kutsatira ndandanda yanga yowerengera Baibulo tsiku ndi tsiku.”

  • Musamagwe ulesi. Ngati pachitika zadzidzidzi ndipo mwalephera kuwerenga Baibulo pa nthawi imene mumawerenga, muziwerengabe mavesi ochepa musanagone. Mukhoza kupindulabe ngakhale mutangowerenga mavesi ochepa okha patsiku.—1 Pet. 2:2.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena