Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yb17 tsamba 105
  • Ndinkafunitsitsa Nditasintha Zochita Zanga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ndinkafunitsitsa Nditasintha Zochita Zanga
  • Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2017
  • Nkhani Yofanana
  • Ndinkaganiza Kuti Zinthu Zikundiyendera
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2017
  • Ndinakopeka ndi Mboni za Yehova
    Galamukani!—2010
  • Baibulo Limasintha Anthu
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Baibulo Limasintha Anthu
    Nsanja ya Olonda—2012
Onani Zambiri
Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2017
yb17 tsamba 105

GEORGIA

Ndinkafunitsitsa Nditasintha Zochita Zanga

Davit Samkharadze

  • CHAKA CHOBADWA 1967

  • CHAKA CHOBATIZIDWA 1989

  • MBIRI YAKE Anatumikirapo monga woyang’anira dera. Kuyambira mu 2013, wakhala akuphunzitsa masukulu osiyanasiyana ophunzitsa Baibulo.

M’bale Davit Samkharadze akuphunzitsa kalasi yophunzitsa Baibulo

MU 1985, ndili ndi zaka 18, boma la Soviet Union linandiuza kuti ndikamenye nawo nkhondo. Kunena zoona sindinkafuna kumenya nawo nkhondo chifukwa ndinkaona kuti asilikali amakonda kuchita zinthu zankhanza komanso zopanda chilungamo. Pansi pamtima ndinkati, ‘Sindikufuna kukhala ngati anthu amenewa.’ Kenako ndinapitabe kukamenya nkhondo koma ndinkaona kuti ndikulephera kuchita zinthu zabwino zomwe ndinkafuna kuchita. Kunena zoona, ndinkafunitsitsa nditasintha zochita zanga.

Nditamaliza kugwira ntchito ya usilikali, ndinabwereranso kwathu. Tsiku lina chakumadzulo titamaliza kuchita phwando limene tinakonza, ndinapempha Mulungu kuti andithandize kusintha moyo wanga. Tsiku lotsatira pamene ndinkapita kuntchito, ndinadzera kunyumba kwa azakhali anga, omwe anali a Mboni za Yehova. Nditalowa m’nyumba, ndinapeza anthu akuchita Phunziro la Buku la Mpingo. Anthuwo anandilandira bwino, moti ndinaganiza zokhala pansi kuti ndimve zimene ankakambirana.

Atandipempha kuti ndiziphunzira Baibulo, ndinavomera ndipo patangotha miyezi 6, ndinabatizidwa. Ndimaona kuti Yehova anandithandiza kuti ndikhale munthu wabwino, chinthu chomwe sindikanakwanitsa pandekha.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena