Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 48
  • Kodi Mulungu Analenga Mdyerekezi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mulungu Analenga Mdyerekezi?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Kodi Mulungu Analenga Mdyerekezi?
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Mdani wa Moyo Wosatha
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
  • Mdyerekezi Alipo Si Nthano Chabe
    Nsanja ya Olonda—2001
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 48
Mngelo wosamvera amene anakhala Mdyerekezi

Kodi Mulungu Analenga Mdyerekezi?

Yankho la m’Baibulo

Baibulo limasonyeza kuti Mulungu sanalenge Mdyerekezi. Koma iye analenga munthu amene kenako anadzakhala Mdyerekezi. Ponena za Mulungu, Baibulo limati: “Ntchito yake ndi yangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika, amene sachita chosalungama. Iye ndi wolungama ndi wowongoka.” (Deuteronomo 32:3-5) Tikaona mawu amenewa, tingadziwe kuti nthawi inayake Satana Mdyerekezi anali m’modzi wa ana auzimu a Mulungu, kapena kuti mngelo wolungama ndiponso wangwiro.

Palemba la Yohane 8:44, Yesu ananena kuti Mdyerekezi “sanakhazikike m’choonadi.” Mfundo imeneyi ikusonyeza kuti nthawi inayake Satana anali m’choonadi ndipo sankachita zoipa.

Komabe, mofanana ndi angelo onse komanso anthu amene Yehova analenga, mngelo amene anadzakhala Satana anali ndi ufulu wosankha kuchita zabwino kapena zoipa. Popeza iye anasankha kutsutsana ndi Mulungu ndiponso kunyengerera Adamu ndi Hava kuti akhale kumbali yake, iye anasankha yekha kukhala Satana, dzina lomwe limatanthauza “Wotsutsa.”—Genesis 3:1-5; Chivumbulutso 12:9.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena