Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 29
  • Kodi Ndizipemphera kwa Anthu Oyera Mtima?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Ndizipemphera kwa Anthu Oyera Mtima?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Oyera Mtima
    Kukambitsirana za m’Malemba
  • Kodi N’zoyenera Kupemphera kwa Oyera Mtima?
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Kodi Tiyenera Kupemphera kwa “Oyera”?
    Galamukani!—2010
  • Kodi Anthu Oyera Mtima Enieni Angakuthandizeni Bwanji?
    Nsanja ya Olonda—2002
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 29

Kodi Ndizipemphera kwa Anthu Oyera Mtima?

Yankho la m’Baibulo

Ayi. Baibulo limatiuza kuti tizipemphera kwa Mulungu yekha, m’dzina la Yesu. Yesu anauza ophunzira ake kuti: “Chifukwa chake pempherani inu chomwechi: Atate wathu wa Kumwamba, Dzina lanu liyeretsedwe.” (Mateyu 6:9, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu) Yesu anauza ophunzira ake kuti azipemphera kwa Mulungu yekha, osati kwa anthu oyera mtima, angelo kapena wina aliyense.

Yesu anauzanso otsatira ake kuti: “Ine ndine njira, ndi choonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.” (Yohane 14:6, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu) Mulungu anapereka udindo kwa Yesu yekha woti azitichonderera kwa iye.—Aheberi 7:25.

Kodi pali vuto ngati nditamapemphera kwa Mulungu komanso kwa anthu oyera mtima?

Mulungu anapatsa anthu ake Malamulo Khumi. M’lamulo lina, iye ananena kuti: “Ine Yehova Mulungu wako ndiri Mulungu wansanje.” (Ekisodo 20:5, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu) Kodi mawu akuti Yehova ndi “Mulungu wansanje” akutanthauza chiyani? Mawu a m’munsi palembali mu Baibulo la Dziko Latsopano amanena kuti iye ndi “Mulungu wosalola aliyense kupikisana naye.” Mulungu amafuna kuti anthu azilambira ndiponso kupemphera kwa iye yekha.—Yesaya 48:11.

Mulungu sasangalala tikamapemphera kwa milungu ina kapena anthu ena, ngakhale kwa anthu oyera mtima kapenanso angelo. Pa nthawi ina, mtumwi Yohane ankafuna kulambira mngelo, koma mngeloyo anamuletsa n’kumuuza kuti: “Usatero; ine ndine kapolo mnzako, ndi mnzawo wa abale ako akukhala nawo umboni wa Yesu; lambira Mulungu.”—Chivumbulutso 19:10, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena