26 Koma Mose anati: “Sizoyenera kuchita zimenezo, chifukwa nyama zomwe tingapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu zingakhale zonyansa kwa Aiguputo.+ Kodi Aiguputo sadzatiponya miyala akationa tikupereka nsembe nyama zimene amaziona kuti ndi zonyansa?