39 Ndiyeno anapanga zovala zolukidwa bwino zoti azivala potumikira mʼmalo oyera. Zovalazo anazipanga pogwiritsa ntchito ulusi wabuluu, ubweya wa nkhosa wapepo ndi ulusi wofiira kwambiri.+ Anapanga zovala zopatulika za Aroni+ mogwirizana ndi zimene Yehova analamula Mose.