34 Kenako Sauli anati: “Pitani mukauze anthu kuti, ‘Aliyense abweretse ngʼombe yake yamphongo ndi nkhosa ndipo adzaziphere pano kenako nʼkudya. Musachimwire Yehova podya nyama pamodzi ndi magazi ake.’”+ Choncho usiku umenewo, aliyense anabweretsa ngʼombe yake yamphongo nʼkuiphera pamenepo.