16 Wachitazi si zabwino. Ndikulumbira mʼdzina la Yehova, Mulungu wamoyo, anthu inu mukuyenera kufa chifukwa mwalephera kuyangʼanira mbuye wanu, yemwe ndi wodzozedwa wa Yehova.+ Ndiye tayangʼanani! Kodi mkondo wa mfumu ndi jagi yadothi ya madzi+ zimene zinali chakumutu kwake zili kuti?”