25 Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti: ‘Pa tsiku limenelo chikhomo chimene chinakhomedwa pamalo okhalitsa chidzachotsedwa.+ Chidzadulidwa ndipo chidzagwa pansi. Katundu amene anapachikidwa pamenepo adzagwa pansi nʼkuwonongeka, chifukwa Yehova ndi amene wanena zimenezi.’”