16 Tikumva nyimbo zikuimbidwa kuchokera kumalekezero a dziko kuti:
“Ulemelero upite kwa Wolungamayo.”+
Koma ine ndikuti: “Ndatheratu! Ndatheratu ine!
Mayo ine! Anthu akupusitsa anzawo komanso kuwachitira zachinyengo.
Iwo akupitirizabe kuchitira anzawo zachinyengo ndi kuwapusitsa.”+