14 Pali munthu amene ntchito yake ndi yogwetsa mitengo ya mkungudza.
Iye amasankha mtengo wamtundu winawake, mtengo waukulu kwambiri,
Ndipo amausiya kuti ukule nʼkukhwima pakati pa mitengo yamʼnkhalango.+
Iye amadzala mtengo wa paini ndipo mvula imaukulitsa.