2 “Dzanja langa ndi limene linapanga zinthu zonsezi,
Ndipo izi ndi zimene zinachitika kuti zonsezi zikhalepo,” akutero Yehova.+
“Choncho ine ndidzayangʼana munthu ameneyu,
Ndidzayangʼana munthu wodzichepetsa ndiponso wosweka mtima amene amadera nkhawa mawu anga.+