32 Kenako Yeremiya anatenga mpukutu wina nʼkupatsa Baruki mlembi,+ mwana wa Neriya. Baruki analembamo mawu onse amene Yeremiya anamuuza, amene anali mumpukutu umene Yehoyakimu mfumu ya Yuda inawotcha.+ Mumpukutumo anawonjezeramo mawu ena ambiri ochokera kwa Mulungu.