6 Choncho losera zokhudza dziko la Isiraeli ndipo uuze mapiri, zitunda, mitsinje ndi zigwa kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ineyo ndidzalankhula mwaukali ndiponso nditakwiya kwambiri chifukwa chakuti anthu a mitundu ina akhala akukunyozani.”’+