16 Zipinda za alondazo komanso zipilala zimene zinali mʼmbali mwa zipindazo zinali ndi mawindo amene anali ndi mafelemu aakulu mkati koma aangʼono kunja+ kuzungulira kanyumba konseko. Mkati mwa makonde munalinso mawindo mbali zonse ndipo pazipilala zamʼmbali panali zithunzi za mtengo wa kanjedza.+