36 Pa nthawi imeneyo nzeru zanga zinabwerera ndipo ndinalandiranso ufumu wanga ndi ulemerero wake wonse komanso ulemu.+ Nduna zanga zikuluzikulu ndi anthu olemekezeka anayamba kufunsiranso malangizo kwa ine. Ndinabwezeretsedwa pampando wanga wachifumu ndipo anthu anayamba kundipatsa ulemu waukulu.