9 Ndinaona Yehova+ ataima pamwamba pa guwa lansembe ndipo anati: “Menya mutu wa chipilala ndipo maziko ake adzagwedezeka. Udulenso mitu ya zipilala zonse ndipo anthu otsalawo ndidzawapha ndi lupanga. Aliyense amene adzathawa ndidzamuphabe, aliyense amene adzayese kuthawa sadzapulumuka.+