5 Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Ambuye Wamkulu Koposa, ndi amene amakhudza dziko lapansi,
Moti limasungunuka+ ndipo onse okhala mmenemo adzalira.+
Dziko lonse lidzasefukira ngati mtsinje wa Nailo,
Ndipo kenako lidzaphwa ngati mtsinje wa Nailo wa ku Iguputo.+