3 Uwauze kuti, ‘M’mibadwo yanu yonse munthu aliyense wodetsedwa mwa ana anu, amene adzayandikira zinthu zopatulika, zimene ana a Isiraeli azipatula kuti azipereke nsembe kwa Yehova,+ munthu ameneyo aziphedwa kuti asakhalenso pamaso panga. Ine ndine Yehova.