19 “Ukaiwala mtolo wa tirigu pokolola m’munda wako,+ usabwerere kukatenga mtolowo. Uzisiyira mlendo wokhala m’dziko lanu, mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye.+ Uzichita zimenezi kuti Yehova Mulungu wako akudalitse pa chilichonse chimene dzanja lako likuchita.+