5 Chotero anasonkhanitsa ansembe+ ndi Alevi n’kuwauza kuti: “Pitani m’mizinda ya Yuda kukasonkhanitsa ndalama kwa Aisiraeli onse kuti muzikonzera+ nyumba ya Mulungu wanu chaka ndi chaka.+ Chitani zimenezi mwachangu.” Koma Aleviwo sanachite zimenezo mwachangu.+