11 “Inu nonse amene mukuyatsa moto, amene mukuchititsa kuti uziwala n’kumathetheka, yendani m’kuwala kwa moto wanu, ndipo yendani pakati pa malawi a moto wothetheka umene mwayatsawo. Mudzalandira izi kuchokera m’dzanja langa: Mudzagona pansi mukumva ululu woopsa.+