3 “Moponderamo mphesa ndapondapondamo ndekha,+ chifukwa palibe munthu amene anali nane wochokera pakati pa mitundu ya anthu. Iwo ndawapondaponda mu mkwiyo wanga,+ ndipo ndawapondereza mu ukali wanga.+ Magazi awo awazikira pazovala zanga,+ ndipo ndaipitsa zovala zanga zonse.