20 “Kumeneko sikudzakhalanso mwana woyamwa wongokhala ndi moyo masiku ochepa okha,+ kapena nkhalamba imene sidzakwanitsa masiku ake.+ Pakuti ngakhale munthu womwalira ali ndi zaka 100 adzaoneka ngati kamnyamata, ndipo wochimwa, ngakhale ali ndi zaka 100, temberero lidzamugwera.+