6 Yehova anapitiriza kulankhula nane m’masiku a Mfumu Yosiya kuti:+ “‘Kodi waona zimene Isiraeli wosakhulupirikayu akuchita?+ Akupita kuphiri lililonse lalitali+ ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu wa masamba ambiri obiriwira+ kuti akachite uhule kumeneko.+