18 “‘Amenewa ndiwo maloto amene ine Mfumu Nebukadinezara ndinalota. Tsopano iwe Belitesazara umasulire malotowa, pakuti amuna ena onse anzeru a mu ufumu wanga alephera kuwamasulira.+ Koma iwe ungathe kuwamasulira chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.’+