3 Pamenepo Yona ananyamuka n’kulowera ku Tarisi,+ kuthawa Yehova.+ Kenako anafika ku Yopa+ ndipo kumeneko anapeza chombo chopita ku Tarisi. Iye analipira malipiro a ulendowo n’kukwera chombocho kuti apite ku Tarisi limodzi ndi anthu amene anali m’chombomo, kuthawa Yehova.