Mawu a M'munsi
Mawu ake enieni, “kulemera.” Mawu achiheberi otanthauza “katundu wolemetsa” ali ndi matanthauzo awiri. Panopa m’lembali akutanthauza uthenga wamphamvu wochokera kwa Mulungu, koma pamalo otsatira m’lemba lomweli akutanthauza kuti anthuwo anali katundu wolemetsa kwa Mulungu. Choncho poyankha, Yeremiya anagwiritsa ntchito mawuwa chifukwa cha matanthauzo ake awiriwa.