Mawu a M'munsi
b Ngati munayesapo kusuta fodya mseri, chonde funani chithandizo mwakuwadziŵitsa makolo anu vutolo. (Miyambo 28:13) Iwo angakwiye atadziŵa vuto lanu. Koma ngati iwo ndi Akristu, adzasumika malingaliro pa kukuthandizani kupeŵa kubwereza cholakwacho kukwiya kwawo koyamba kutatha. Oyang’anira mumpingo wakumaloko wa Mboni za Yehova angakhalenso othandiza kwambiri ndi achilimbikitso kwa inu ponena za nkhaniyi.—Yakobo 5:14, 15.