Mawu a M'munsi
a Alipo malo ambiri opereka chithandizo, zipatala, ndi maprogramu othandiza amene angapereke malangizo pazimenezo. Galamukani! panopa sikusankhira munthu aliyense njira yakuchiritsa yakutiyakuti. Amene amafuna kutsatira malamulo amakhalidwe abwino a Baibulo ayenera kusamala kusadziloŵetsa m’zochita zimene zikawapangitsa kulolera molakwa malamulo amakhalidwe abwino Amalemba. Munthu yemwe ndimmodzi wa Mboni za Yehova adzapeza zitsogozo zothandiza mu Nsanja ya Olonda ya October 1, 1983, masamba 9-13.