Mawu a M'munsi
b Ndithudi, makolo ayenera kusambitsa ndi kuveka ana aang’ono zovala, ndipo panthaŵiyo makolo amasambitsa ziŵalo zamtseri zimenezo. Koma phunzitsani ana anu akali aang’ono kusamba okha; akatswiri ena osamalira za ana amanena kuti iwo ayenera kuphunzira kusambitsa ziŵalo zawo zamtseri pofika usinkhu wa zaka zitatu ngati kutheka.