Mawu a M'munsi
a Mboni za Yehova zimene zasankha utumiki Wachikristu monga ntchito yawo ndi kutumikira monga atumiki anthaŵi yonse zili ndi mwaŵi wa kuchita kosi ya milungu iŵiri ya Sukulu ya Utumiki Waupainiya. Ena pambuyo pake amayeneretsedwa kulembetsa kosi ya miyezi isanu ya maphunziro aumishonale ochititsidwa ndi Sukulu ya Baibulo ya Watchtower ya Gileadi kuwakonzekeretsa monga amishonale.