Mawu a M'munsi
a Pamene kuli kwakuti liwulo “Mwini America” tsopano limakondedwa ndi ena, nalonso liwu lakuti “Mwiindiya” limagwiritsiridwa ntchito m’mabuku ambiri. Tidzagwiritsira ntchito mawu ameneŵa mosinthanasinthana. Liwu lakuti “Mwiindiya” ndilo dzina lolakwika loperekedwa kwa nzikazo ndi Columbus, amene anaganiza kuti anali atafika ku India pamene anafika kumalo amene tsopano timawadziŵa kuti West Indies.