Mawu a M'munsi
a Chosangalatsa nchakuti mabungwe ofuna kutetezera nyama zambiri kuti zisasoloke, amati lamulo lawo lili ngati “lamulo la Nowa,” chifukwa Nowa analangizidwa kuloŵetsa m’chingalaŵa nyama “ziŵiriziŵiri za mtundu wawo.” (Genesis 6:19) Wophunzira za nyama, David Ehrenfeld, anati: “Timaona kuti [nyama], zoti zakhala nthaŵi yaitali m’nkhalango, zili nawo ufulu wosatsutsidwa wakukhalapobe.”