Mawu a M'munsi
b Magazini yotchedwa New Scientist inanena kuti mbewu za ku Ulaya za sugar beet zimene “anazisintha chilengedwe chake kuti zisamafe ndi mankhwala ophera udzu m’munda zasinthanso pazokha kuti zisamafe ndi mankhwala amtundu winanso.” Mbewuzi zinasintha pamene zinalandira ufa wochokera ku mtundu wina wa mbewuzi umene unazisintha kuti zisamafe ndi mankhwala ena ophera udzu m’munda. Asayansi ena akuda nkhaŵa kuti n’kutheka kuti kugwiritsa ntchito kwambiri mbewu zotere kungapangitse kuti pakhale mtundu wa tchire la m’munda losamva mankhwala.