Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO

Mawu a M'munsi

a Palinso nkhani ina yotere yakuti “Kodi Ndege N’zodalirika Motani?” imene mungathe kuipeza mu Galamukani! ya pa September 8 1999.

[Bokosi/Chithunzi pamasamba 10, 11]

MALANGIZO ENA OTHANDIZA KUTI MUYENDE BWINO

Kwerani ndege zosaima m’njira. Ngozi zambiri zimachitika ndege ikayamba kuthamanga pansi, ikamasiya nthaka kapenanso ikamatera. Mukakwera ndege yosaima paliponse mumachepetsa tsoka lokumanizana ndi ngozi zimenezi.

Kwerani ndege zazikulu. Ndege zokwera anthu oposa 30 nthaŵi zambiri pozipanga ndiponso pozipatsa chilolezo choti ziziyenda, amatsatira malamulo okhwima kwambiri poyerekezera ndi ndege zazing’onopo. Komanso ngati patachitika ngozi yaikulu, ngakhale kuti sizichitikachitika, m’ndege zazikulu m’posavuta kuti anthu apaulendo apulumuke.

Mvetserani bwino malangizo operekedwa ndege isananyamuke. Ngakhale kuti malangizo ameneŵa amakhala ngati obwerezabwereza, makomo apafupi kwambiri otulukira pangozi amakhala osiyanasiyana malingana ndi ndege yake ndiponso mpando umene mwakhala.

Musaike katundu wolemera pamwamba. Ndege ikakumana ndi chimphepo katundu amalephera kukhazikika m’malo oikapo katundumo, choncho ngati muli ndi katundu winawake amene angakuvuteni kum’loŵetsa mmenemu, mum’perekeretu pasadakhale kuti akamuike kosungira katundu wotere.

Mukakhala pansi lamba wanu azikhala chimangire. Kumanga lamba mukakhala pansi kumakutetezani ndege ikakumana ndi chimphepo.

Mvetserani zimene okuyang’anirani m’ndegemo akunena. Chifukwa chachikulu chimene amaikira anthu oyang’anira apaulendo m’ndege n’chakuti akuthandizeni paulendo wanuwo. Motero ngati munthu wina wotere atakuuzani kuti muchite chinachake, chitani kaye chinthucho n’kumafunsa bwino mafunso pambuyo pake.

Musatenge zinthu zilizonse zangozi. Pali zinthu zambiri zimene zingathe kuchititsa ngozi zimene siziloledwa m’ndege koma zina n’zosachita kulira kufunsa. Mungathe kudziŵa panokha kuti musatenge zinthu monga petulo, zinthu zokhala ndi asidi, gasi wakupha, ndi zinthu zina zotere pokhapokha ngati kampani ya ndegeyo itavomereza ndipo ngati atazinyamulira m’chinthu choyenera.

Osamwa kwambiri. Mukamwa moŵa, umakula mphamvu mukapita m’mwamba kuposa mukakhala pansi. Nthaŵi zonse ndi bwino kusamwetsa moŵa pena paliponse, kaya ndi m’mwambamo ngakhalenso pansi pompano.

Khalani tcheru. Ngati zosaonekaoneka zija zitachitika mwadzidzidzi, monga zakuti nonse mutulukemo m’ndegemo mwamsanga poopa chinachake, muyenera kutsatira malangizo a anthu oyang’anira apaulendo aja komanso anthu ena ogwira ntchito m’ndegemo ndipo tulukanimo mwamsanga.

[Mawu a Chithunzi]

Zachokera ku Airsafe.com

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena