Mawu a M'munsi
a Si timadzi tokhati timene timawononga mwana yemwe ali m’mimba mwa amayi ake. Palinso fodya, mowa, ndi mankhwala ozunguza bongo omwe angachite chimodzimodzi. Ndi bwino kuti azimayi oyembekezera azipewa chilichonse chowononga. Komanso, ndi bwino kwambiri kufunsa dokotala kuti mudziŵe ngati mankhwala opatsa mayi woyembekezera angakhale oopsa kwa mwana yemwe ali m’mimba mwake.