Mawu a M'munsi
b Akuluakulu ena amagona ana pofuna kukhutiritsa zilakolako zawo. Iwo kawirikawiri amachita zimene Baibulo limazitcha dama, kapena kuti por·neiʹa, zomwe zimaphatikizapo kuchita zinthu monga kuwaseweretsa maliseche, kuwagona, ndiponso kuwagona m’kamwa kapena kumatako. Zina mwa nkhanza zomwe akuluakulu amachita kwa ana ndi kuwasisita mabere, kuwanyengerera kuti achite nawo zopusa, kuwaonetsa zinthunzi zolaula, kuwaonera, ndiponso kuwaonetsa maliseche. Baibulo limaletsa zimenezi ndipo limazitcha ‘khalidwe lotayirira, lonyansa kapena ladyera.’—Agalatiya 5:19-21; Aefeso 4:19.