Mawu a M'munsi
a Panali zivomezi zokwanira zisanu pakati pa 1914 ndi 1918 zimene kulemera kwake kunafika 8 kapena kuposerapo pa sikelo yopimira zivomezi ya Richter—zamphamvu kwambiri koposa chivomezi cha pa Abruzzi. Komabe, zivomezi zimenezi zinachitikira kumalo akutali kwambiri a dziko lapansi, ndipo motero sizinadziŵidwe kwambiri mofanana ndi chivomezi cha mu Italiya.5