Mawu a M'munsi
c Zikuoneka kuti zikhulupiriro za Ababulo zinawonjezera kuopsa kwa chozizwitsacho. Buku lakuti Babylonian Life and History limati: “Kuwonjezera pa milungu yambiri imene Ababulo anailambira, tikuona kuti anakhulupiriranso kwambiri mizimu, mwakuti mapemphero awo oitsutsa ndi matemberero zimapanga gawo lalikulu kwambiri la mabuku awo achipembedzo.”