Mawu a M'munsi
a “Nthawi yobwezeretsa zinthu zonse” inayamba pamene Ufumu wa Mesiya unakhazikitsidwa komanso pamene mbadwa ya Mfumu Davide, yemwe anali wokhulupirika, inakhala Mfumu. Yehova analonjeza Davide kuti mmodzi wa mbadwa zake adzalamulira mpaka kalekale. (Salimo 89:35-37) Koma Ababulo atawononga Yerusalemu mu 607 B.C.E., palibe mbadwa ya Davide iliyonse imene inakhala pampando wachifumu wa Mulungu. Yesu, amene anabadwa monga wolowa ufumu wa Davide, anakhala Mfumu yomwe Mulungu analonjeza kalekale, pamene anapatsidwa Ufumu kumwamba.